14. Pamenepo Danieli anabweza mau a uphungu wanzeru kwa Arioki mkuru wa olindirira a mfumu, adaturukawo kukapha eni nzeru a ku Babulo;
15. anayankha nati kwa Arioki mkuru wa olindirira a mfumu, Cilamuliro ca mfumu cifulumiriranji? Pamenepo Arioki anadziwitsa Danieli cinthuci.
16. Nalowa Danieli, nafunsa mfumu amuikire nthawi, kuti aululire mfumu kumasulira kwace.