Danieli 11:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Koma iye amene amdzera kulimbana naye adzacita cifuniro cace ca iye mwini; palibe wakulimbika pamaso pace; ndipo adzaima m'dziko lokometsetsalo, ndi m'dzanja mwace mudzakhala cionongeko.

17. Ndipo adzalimbitsa nkhope yace, kudza ndi mphamvu ya ufumu wace wonse, ndi oongoka mtima pamodzi naye; ndipo adzacita cifuniro cace, nadzampatsa mwana wamkazi wa akazi kumuipitsa; koma mkaziyo sadzalimbika, kapena kubvomerezana naye.

18. Pambuyo pace adzatembenuzira nkhope yace kuzisumbu, nadzalanda zambiri; koma kalonga wina adzaleketsa kunyoza kwace adanyoza nako; inde adzambwezera yekha kunyoza kwace.

19. Pamenepo adzatembenuzira nkhope yace ku malinga a dziko lace lace; koma adzakhumudwa, nadzagwa osapezedwanso.

Danieli 11