11. Ndidza msanga; gwira cimene uli naco, kuti wina angalande korona wako.
12. Iye wakulakika, ndidzamyesa iye mzati wa m'Kacisi wa Mulungu wanga, ndipo kuturuka sadzaturukamonso; ndipo ndidzalemba pa iye dzina la Mulungu wanga, ndi dzina la mzinda wa Mulungu wanga, la Yerusalemu watsopano, wotsika m'Mwamba, kucokera kwa Mulungu wanga; ndi dzina langa latsopano.
13. Iye wakukhala nalo khutu amve cimene Mzimu anena kwa Mipingo.
14. Ndipo kwa mngelo wa Mpingo wa ku Laodikaya lemba:Izi anena Amenyo, mboni yokhulupirika ndi yoona, woyamba wa cilengo ca Mulungu:
15. Ndidziwa nchito zako, kuti suli wozizira kapena wotentha: mwenzi utakhala wozizira kapena wotentha.