18. Ndipo kwa mngelo wa Mpingo wa ku Tiyatira lemba:Izi azinena Mwana wa Mulungu, wakukhala nao maso ace ngati lawi la moto, ndi mapazi ace ngati mkuwa wonyezimira:
19. 1 Ndidziwa nchito zako, ndi cikondi, ndi cikhulupiriro, ndi utumiki, ndi cipiriro cako, ndi kuti nchito zako zotsiriza cicuruka koposa zoyambazo.
20. Komatu ndiri nako kotsutsana ndi iwe, cuti ulola mkazi 2 Yezebeli, wodzieha zekha mneneri; ndipo aphunzitsa, nasokeretsa akapolo anga, kuti acite cigololo ndi kudya zoperekedwa nsenbe kwa mafano.
21. Ndipo ndanpatsa iye nthawi kuti alape; koma safuna kulapa kusiyana naco cigololo cace.