Aroma 9:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. ndiwo Aisrayeli; ali nao umwana, ndi ulemerero, ndi mapangano, ndi kupatsa kwa malamulo, ndi kutumikira m'kacisi wa Mulungu, ndi malonjezo;

5. a iwo ali makolo, ndi kwa iwo anacokera Kristu, monga mwa thupi, ndiye Mulungu wa pamwamba pa zonse wolemekezeka ku nthawi zonse. Amen.

6. Koma sikuli ngati mau a Mulungu anakhala cabe ai. Pakuti onse akucokera kwa a Israyeli siali Israyeli;

7. kapena cifukwa ali mbeu ya Abrahamu, siali onse ana; koma anati, Mwa Isake, mbeu yako idzaitanidwa.

Aroma 9