Aroma 7:3-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo cifukwa cace, ngati iye akwatiwa ndi mwamuna wina, pokhala mwamuna wace wamoyo, adzanenedwa mkazi wacigololo; koma mwamunayo akafa, iye amasulidwa ku lamuloli; cotero sakhala wacigololo ngati akwatiwa ndi mwamuna wina.

4. Cotero, abale anga, inunso munayesedwa akufa ku cilamulo ndi thupi la Kristu; kuti mukakhale ace a wina, ndiye amene anaukitsidwa kwa akufa, kuti ife timbalire Mulungu zipatso,

5. Pakuti pamene tinali m'thupi, zilakolako za macimo, zimene zinali mwa cilamulo, zinalikucita m'ziwalo zathu, kuti zibalire imfa zipatso,

Aroma 7