Aroma 7:23-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. koma ndiona lamulo lina m'ziwalo zanga, lirikulimbana ndi lamulo la mtima wanga, ndi kundigonjetsa kapolo wa lamulo la m'ziwalo zanga.

24. Munthu wosauka ine; adzandilanditsa ndani m'thupi la imfa iyi?

25. Ndiyamika Mulungu, mwa Yesu Kristu Ambuye wathu. Ndipo cotero ine ndekha ndi mtimatu nditumikira cilamulo ca Mulungu; koma ndi thupi nditumikira lamulo la ucimo.

Aroma 7