19. Ndipo iye osafoka m'cikhulupiriro sanalabadira thupi lace, ndilo longa ngati lakufa pamenepo, (pokhala iye ngati zaka makumi khumi), ndi mimba ya Sara idaumanso;
20. ndipo poyang'anira lonjezo la Mulungu sanagwedezeka cifukwa ca kusakhulupirira, koma analimbika m'cikhulupiriro, napatsa Mulungu ulemu,
21. nakhazikikanso mumtima kuti, o cimene iye analonjeza, anali nayonso mphamvu yakucicita.