Aroma 3:8-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Ndipo tilekerenji kunena, Ticite zoipa kuti zabwino zikadze (monganso ena atinamiza ndi kuti timanena)? Kulanga kwa amenewo kuli kolungama.

9. Ndipo ciani tsono? kodi tiposa ife? Iai ndithu; pakuti tidawaneneza kale Ayuda ndi Ahelene omwe, kuti onsewa agwidwa ndi ucimo;

10. monga kwalembedwa,Palibe mmodzi wolungama, inde palibe mmodzi;

11. Palibe mmodzi wakudziwitsa, Palibe mmodzi wakuloodola Mulungu;

12. Onsewa apatuka, pamodzi akhala opanda pace;Palibe mmodzi wakucita zabwino, inde, palibe mmodzi ndithu.

Aroma 3