Aroma 3:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Msatero ai. Ngati kotero, Mulungu adzaweruza bwanji mlandu wa dziko lapansi?

7. Pakuti ngati coonadi ca Mulungu cicurukitsa ulemerero wacecifukwa ca bodza langa, nanga inenso ndiweruzidwa bwanji monga wocimwa?

8. Ndipo tilekerenji kunena, Ticite zoipa kuti zabwino zikadze (monganso ena atinamiza ndi kuti timanena)? Kulanga kwa amenewo kuli kolungama.

9. Ndipo ciani tsono? kodi tiposa ife? Iai ndithu; pakuti tidawaneneza kale Ayuda ndi Ahelene omwe, kuti onsewa agwidwa ndi ucimo;

10. monga kwalembedwa,Palibe mmodzi wolungama, inde palibe mmodzi;

Aroma 3