Aroma 15:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ife amene tiri olimba tiyenera kunyamula zofoka za opanda mphamvu, ndi kusadzikondweretsa tokha.

2. Yense wa ife akondweretse mnzace, kumcitira zabwino, zakumlimbikitsa.

3. Pakuti Kristunso sanadzikondweretsa yekha; koma monga kwalembedwa, Minyozo ya iwo amene anakuoyoza iwe Inagwa pa Ine,

4. Pakuti zonse zinalembedwa kale zinalembedwa kutilangiza, kuti mwa cipiriro ndi citonthozo ca malembo, tikhale ndi ciyembekezo.

Aroma 15