Amosi 4:11-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndinagubuduza ena mwa inu, monga umo Mulungu anagubuduzira Sodomu ndi Gomora; ndipo inu munali ngati muuni wofumulidwa kumoto; koma simunabwerera kudza kwa Ine, ati Yehova.

12. Cifukwa cace ndidzatero nawe, Israyeli; popeza ndidzakucitira ici, dzikonzeretu kukomana ndi Mulungu wako, Israyeli.

13. Pakuti taona, Iye amene aumba mapiri, nalenga mphepo, nafotokozera munthu maganizo ace, nasanduliza m'mawa ukhale mdima, naponda pa misanje ya dziko lapansi, dzina lace ndiye Yehova Mulungu wamakamu.

Amosi 4