Amosi 1:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za Edomu, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza analondola mphwace ndi lupanga, nafetsa cifundo cace conse, ndi mkwiyo wace unang'amba cing'ambire, nasunga mkwiyo wace cisungire;

12. koma ndidzatumiza moto pa Temani, udzanyeketsa nyumba zacifumu za Bozira.

13. Atero Yehova, Cifukwa ca zolakwa zitatu za ana a Amoni, kapena zinai, sindidzabweza kulanga kwace; popeza anatumbula akazi ali m'pakati a Gileadi, kuti akuze malire ao;

14. koma ndidzayatsa moto pa linga la Raba, udzanyeketsa nyumba zacifumu zace, ndi kupfuula tsiku la nkhondo, ndi namondwe, tsiku la kabvumvulu;

15. ndipo mfumu yao idzalowa kundende, iyo ndi akalonga ace pamodzi, ati Yehova.

Amosi 1