Akolose 1:14-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. amene tiri nao maomboledwe mwa iye, m'kukhululukidwa kwa zocimwa zathu;

15. amene ali fanizo la Mulungu wosaonekayo, wobadwa woyamba wa cilengedwe conse;

16. pakuti mwa iye, zinalengedwa zonse za m'mwamba, ndi za padziko, zooneka ndi zosaonekazo, kapena mipando yacifumu, kapena maufumu, kapena maukulu, kapena maulamuliro; zinthu zonse zinalengedwa mwa iye ndi kwa iye.

17. Ndipo iye ali woyamba wa zonse, ndipo zonse zigwirizana pamodzi mwa iye.

18. Ndipo iye ali mutu wa thupi, Eklesiayo; ndiye ciyambi, wobadwa woyamba woturuka mwa akufa; kuti akakhale iye mwa zonse woyambayamba.

Akolose 1