Ahebri 5:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Monga anenanso mwina,Iwe ndiwe wansembe wa nthawizonseMonga mwa dongosolo la Melikizedeke.

7. Ameneyo, m'masiku a thupi lace anapereka mapemphero ndi mapembedzero pamodzi ndi kulira kwakukuru ndi misozi kwa iye amene anakhoza kumpulumutsa iye muimfa, ndipo anamveka popeza anaopa Mulungu,

8. angakhale anali Mwana, anaphunzira kumvera ndi izi adamva kuwawa nazo;

9. ndipo pamene anakonzeka wamphumphu anakhala kwa onse akumvera iye cifukwa ca cipulumutso cosatha;

10. wochedwa ndi Mulungu mkulu wa ansembe monga mwa dongosolo la Melikizedeke.

Ahebri 5