Ahebri 3:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Potero, abale oyera mtima, olandirana nao maitanidwe akumwamba, lingirirani za Mtumwi ndi. Mkuluwansembe wa cibvomerezo cathu, Yesu;

2. amene anakhala wokhulupirika kwa iye adamuikayo, monganso Mose m'nyumba yace yonse.

3. Pakuti ameneyo wayesedwa woyenera ulemerero woposa Mose, monga momwe iye amene anaimanga nyumba ali nao ulemerero woposa nyumbayi.

Ahebri 3