11. Pakuti iye wakuyeretsa ndi iwo akuyeretsedwa acokera onse mwa mmodzi; cifukwa ca ici alibe manyazi kuwacha iwo abale,
12. ndi kuti,ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga,Pakati pa Mpingo ndidzakuyimbirani.
13. Ndiponso,Ndidzamtama Iye.Ndiponso,Taonani, Ine ndi ana amene Mulungu anandipatsa,
14. Popeza tsono ana ndiwo a mwazi ndi nyama, Iyenso momwemo adalawa nao makhalidwe omwewo kuti mwa imfa akamuononge iye amene anali nayo mphamvu ya imfa, ndiye mdierekezi;
15. nakamasule iwo onse amene, cifukwa ca kuopa imfa, m'moyo wao wonse adamangidwa ukapolo.