Ahebri 10:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Nsembe zopsereza zamphumphu ndi za kwa macimo simunakondwera nazo;

7. Pamenepo ndinati, Taonani, ndafika,(Pamutu pace pa buku palembedwa za Ine)Kudzacita cifuniro canu, Mulungu,

8. Pakunena pamwamba apa, kuti, Nsembe ndi zopereka ndi nsembe zopsereza zamphumphu ndi za kwa macimo simunazifuna, kapena kukondwera nazo (zimene ziperekedwa monga mwa lamulo),

9. pamenepo anati, Taonani, ndafika kudzacita cifuniro canu. Acotsa coyambaco, kuti akaike caciwirico.

10. Ndi cifuniro cimeneco tayeretsedwa mwa copereka ca thupi la Yesu Kristu, kamodzi, kwatha.

Ahebri 10