Ahebri 10:31-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

31. 3 Kugwa m'manja a Mulungu wamoyo nkoopsa.

32. Koma tadzikumbursani masiku akale, m'menemo mutaunikidwa 4 mudapirira citsutsano cacikuru ca zowawa;

33. pena pocitidwa 5 cinthu cooneredwa mwa matonzo ndi zisautso; penanso polawana nao iwo ocitidwa zotere.

34. Pakuti 6 munamva cifundo ndi iwo a m'ndende, ndiponso mudalola mokondwera kulandidwa kwa cuma canu, 7 pozindikira kuti muli naco nokha cuma coposa caeikhalire.

35. Potero musataye kulimbika kwanu, kumene kuli naco cobwezera mphotho cacikuru.

Ahebri 10