Ahebri 10:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. pa njira yatsopano ndi yamoyo, imene adatikonzera, mwa cocinga, ndico thupi lace;

21. ndipo popeza tiri naye wansembe wamkuru wosunga nyumba ya Mulungu;

22. tiyandikire ndi mtima woona, m'cikhulupiriro cokwanira, ndi mitima yathu yowazidwa kuicotsera cikumbu mtima coipa, ndi matupi athu osambitsidwa ndi madzi oyera;

23. tigwiritse cibvomerezo cosagwedera ca ciyembekezo cathu, pakuti wolonjezayo ali wokhulupirika;

24. ndipo tiganizirane wina ndi mnzace kuti tifulumizane ku cikondano ndi nchito zabwino,

Ahebri 10