Agalatiya 5:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndicitanso umboni kwa munthu yense wolola amdule, kuti ali wamangawa kucita cilamulo conse.

4. Mulibe kanthu ndi Kristu, inu amene muyesedwa olungama ndi lamulo; mudagwa posiyana naco cisomo.

5. Pakuti ife mwa Mzimu, kucokera m'cikhulupiriro, tilindira ciyembekezo ca cilungamo,

6. Pakuti mwa Kristu Yesu kapena mdulidwe kapena kusadulidwa kulibe mphamvu; komatu cikhulupiriro cakucititsa mwa cikondi.

7. Munathamanga bwino; anakuletsani ndani kuti musamvere coonadi?

8. Kukopa kumene sikucokera kwa iye anakuitanani.

Agalatiya 5