Agalatiya 3:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Koma cisanadze cikhulupiriro tinasungidwa pomvera lamulo otsekedwa kufikira cikhulupiriro cimene cikabvumbulutsidwa bwino bwino.

24. 1 Momwemo cilamulo cidakhala namkungwi wathu wakutifikitsa kwa Kristu, 2 kuti tikayesedwe olungama ndi cikhulupiriro.

25. Koma popeza cadza cikhulupiriro, sitikhalanso omvera namkungwi.

26. 3 Pakuti inu nonse muli ana a Mulungu, mwa cikhulupiriro ca mwa Yesu Kristu.

Agalatiya 3