Afilipi 4:19-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Koma Mulungu wanga adzakwaniritsa cosowa canu ciri conse monga mwa cuma cace m'ulemerero mwa Kristu Yesu.

20. Ndipo kwa Mulungu ndi Atate wathu kukhale ulemerero ku nthawi za nthawi, Amen.

21. Lankhulani woyera mtima ali yense mwa Kristu Yesu. Abalewo akukhala ndiine alankhula inu.

22. Oyera mtima onse alankhula inu, koma makamaka-fwo a banja la Kaisara.

23. Cisomo ca Ambuye Yesu Kristu cikhale ndi mzimu wanu.

Afilipi 4