Aefeso 6:19-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. ndi ine ndemwe, kuti andipatse mau m'kunditsegulira m'kamwa molimbika, kuti ndizindikiritse anthu cinsinsico ca Uthenga Wabwino,

20. cifukwa ca umene 1 ndiri mtumiki wa m'unyolo, kuti m'menemo ndikalankhule molimbika, monga ndiyenera kulankhula.

21. Koma 2 kuti mukadziwe inunso za kwa ine, zimene ndicita, zinthu zonse adzakuzindikiritsani Tukiko mbale wokondedwayo, ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye;

22. amene ndamtuma kwa inu cifukwa ca icico, kuti mukazindikire za kwa ife, ndi kuti akatonthoze mitima yanu.

23. 3 Mtendere ukhale kwa abale, ndi cikondi, pamodzi ndi cikhulupiriro, zocokera kwa Mulungu Atate, ndi Ambuye Yesu Kristu.

24. Akhale naco cisomo onse akukonda Ambuye wathu Yesu Kristu m'eosaonongeka.

Aefeso 6