Aefeso 5:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Cifukwa cace khalani akutsanza a Mulungu, monga ana okondedwa;

2. ndipo yendani m'cikondi monganso Kristu anakukondani inu, nadzipereka yekha m'malo mwathu, copereka ndi nsembe kwa Mulungu, ikhale pfungo lonunkhira bwino.

3. Koma dama ndi cidetso conse, kapena cisiriro, zisachulidwe ndi kuchulidwa komwe mwa inu, monga kuyenera oyera mtima;

4. kapena cinyanso, ndi kulankhula zopanda pace, kapena zopusa zimene siziyenera; koma makamaka ciyamiko.

Aefeso 5