4. Msilikari sakodwa nazo nchito wamba, kuti akakondweretse iye amene adamlemba usilikari.
5. Koma ngatinso wina ayesana nao m'makani a masewero, sambveka korona ngati sanayesana monga adapangana.
6. Wam'munda wogwiritsitsa nchitoyo ayenera akhale woyamba kulandira zipatsozoo
7. Lingirira cimene ndinena; pakuti Ambuye adzakupatsa cidziwitso m'zonse.
8. Kumbukila Yesu Kristu, wouka kwa akufa, wocokera m'mbeu ya Davide, monga mwa Uthenga Wabwino wanga;