3. Umve zowawa pamodzi nane monga msilikari wabwino wa Kristu Yesu.
4. Msilikari sakodwa nazo nchito wamba, kuti akakondweretse iye amene adamlemba usilikari.
5. Koma ngatinso wina ayesana nao m'makani a masewero, sambveka korona ngati sanayesana monga adapangana.
6. Wam'munda wogwiritsitsa nchitoyo ayenera akhale woyamba kulandira zipatsozoo