2 Timoteo 2:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Umve zowawa pamodzi nane monga msilikari wabwino wa Kristu Yesu.

4. Msilikari sakodwa nazo nchito wamba, kuti akakondweretse iye amene adamlemba usilikari.

5. Koma ngatinso wina ayesana nao m'makani a masewero, sambveka korona ngati sanayesana monga adapangana.

6. Wam'munda wogwiritsitsa nchitoyo ayenera akhale woyamba kulandira zipatsozoo

2 Timoteo 2