2 Samueli 8:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo m'tsogolo mwace Davide anakantha Afilisti, nawagonjetsa; Davide nalanda mudzi wa Metege Ama m'manja mwa Afilisti.

2. Ndipo anakantha Amoabu nawayesa ndi cingwe, nawagonetsa pansi; ndipo anawayesera zingwe ziwiri kupha, ndi cingwe cimodzi cathunthu kusunga ndi moyo. Ndipo Amoabu anakhala anthu a Davide, nabwera: nayo mitulo.

3. Davide anakanthanso Hadadezeri, mwana wa Rehobu, mfumu ya ku Zoba, pomuka iye kukadzitengeranso ufumu wace ku cimtsinje ca Firate.

2 Samueli 8