2 Samueli 7:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Iye adzamangira dzina langa nyumba, ndipo ndidzakhazikitsa cimpando ca ufumu wace ku nthawi zonse.

14. Ndidzakhala atate wace, iye nadzakhala mwana wanga; akacita coipa ndidzamlanga ndi ndodo ya anthu, ndi mikwapulo ya ana a anthu;

15. koma cifundo canga sicidzamcokera iye, monga ndinacicotsera Sauli amene ndinamcotsa pamaso pako.

16. Ndipo nyumba yako ndi ufumu wako zidzakhazikikadi ku nthawi zonse pamaso pako; mpando wacifumu wako udzakhazikika ku nthawi zonse.

17. Monga mwa mau onse awa ndi monga mwa masomphenya onse awa, momwemo Natani analankhula ndi Davide.

2 Samueli 7