14. Maina a iwo anambadwira m'Yerusalemu ndi awa: Samua, ndi Sobabu, ndi Natani, ndi Solomo,
15. ndi Ibara ndi Elisua, ndi Nefegi ndi Yafiya;
16. ndi Elisama ndi Eliada ndi Elifeleti.
17. Koma pamene Afilisti anamva kuti adamdzoza Davide mfumu ya Israyeli, Afilisti onse anakwera kukafuna Davide; ndipo Davide anacimva natsikira kungaka kuja.