2 Samueli 2:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Pomwepo iwo anaimirira naoloka owerengedwa, khumi ndi awiri a kwa Benjamini, ndi Isiboseti mwana wa Sauli, ndi khumi ndi awiri a anyamata a Davide.

16. Ndipo anagwirana munthu yense kugwira mutu wa mnzace, nagwaza ndi lupanga lace m'nthiti mwa mnzaceo Comweco anagwa limodzi; cifukwa cace malo aja anachedwa Dera la Mipeni la ku Gibeoni.

17. Ndipo tsikulo nkhondo inakula ndithu. Ndi Abineri ndi anthu a Israyeli anathawa pamaso pa anyamata a Davide.

18. Ndipo analipo ana atatu a Zeruya, ndiwo Yoabu, Abisai ndi Asaheli. Ndipo Asaheli anali waliwiro ngati nyama ya kuthengo.

2 Samueli 2