2. Ndipo mfumu inanena ndi Ziba, Ulikutani ndi zimenezi? Nati Ziba, Aburuwo ndiwo kuti akaberekepo a pa banja lanu; ndi mitanda ya mikate ndi zipatso za m'dzinja ndizo zakudya za anyamata; ndi vinyoyo akufoka m'cipululu akamweko.
3. Ndipo mfumu inati, Mwana wa mbuye wako ali kuti? Ziba nanena ndi mfumu, Onani, akhala ku Yerusalemu; pakuti anati, Lero nyumba ya Israyeli idzandibwezera ufumu wa atate wanga.
4. Pomwepo mfumu inanena ndi Ziba, Ona, za Mefiboseti zonse ziri zako. Ndipo Ziba anati, Ndikulambirani, mundikomere mtima, mbuye wanga mfumu.
5. Ndipo pakufika mfumu Davide ku Bahurimu, onani, panaturuka pamenepo munthu wa banja la nyumba ya Sauli, dzina lace ndiye Simeyi, mwana wa Gera; iyeyu anaturukako, nayenda natukwana.
6. Ndipo iye anaponya miyala Davide ndi anyamata onse a mfumu Davide, angakhale anthu onse ndi ngwazi zonse zinali kudzanja lamanja ndi ku dzanja lamanzere kwace.
7. Ndipo anatero Simeyi pakutukwana, Coka, coka, munthu wa mwazi iwe, woipa iwe;