2 Samueli 16:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndiponso ndidzatumikira yani? si pamaso pa mwana wace nanga? monga ndinatumikira pamaso pa atate wanu, momwemo ndidzakhala pamaso panu,

20. Pomwepo Abisalomu ananena ndi Ahitofeli, Upangire cimene ukuti rikacite.

21. Ndipo Ahitofeli ananena ndi Abisalomu, Mulowe kwa akazi ang'ono a atate wanu amene iye anawasiya kuti asunge nyumbayo; ndipo Aisrayeli onse adzamva kuti atate wanu aipidwa nanu; pomwepo manja a onse akukhala nanu adzalimba.

22. Comweco iwo anayalira Abisalomu hema pamwamba pa nyumba; ndipo Abisalomu analowa kwa akazi ang'ono a atate wace pamaso pa Aisrayeli onse.

2 Samueli 16