2 Samueli 13:33-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. Cifukwa cace tsono mfumu mbuye wanga asasauke mtima ndi cinthuci, ndi kuganiza kuti ana amuna onse a mfumu afa; pakuti Amnoni yekha wafa.

34. Koma Abisalomu anathawa. Ndipo mnyamata wakudikira anatukula maso ace nayang'ana, ndipo onani, m'mbuyo mwace anthu ambiri analikubwera m'njira yolambalala phiri.

35. Ndipo Jonadabu ananena ndi mfumu, Onani, ana amuna a mfumu afika; monga ananena mnyamata wanu, momwemo.

36. Ndipo kunali pakutsiriza iye kulankhula, onani, pomwepo ana amuna a mfumu anafika, nakweza mau ao, nalira misozi; ndi mfumu yomwe ndi anyamata ace analira ndi kulira kwakukuru ndithu.

2 Samueli 13