1. Ndipo kunali, zitatha zaka makumi awiri m'mene anamanga nyumba ya Yehova, ndi nyumba yace yace,
2. Solomo anamanga midzi imene Huramu adampatsa, nakhalitsamo ana a Israyeli.
3. Ndipo Solomo anamuka ku Hamati Zoba, naugonjetsa.
4. Ndipo anamanga Tadimori m'cipululu, ndi midzi yonse yosungiramo cuma, imene anaimanga m'Hamati.
5. Anamanganso Betihoroni wa kumtunda, ndi Betihoroni wa kunsi, midzi ya malinga yokhala nao malinga, zitseko, ndi mipiringidzo;