2 Mbiri 6:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo tsopano, Yehova Mulungu wa Israyeli, msungireni mtumiki wanu Davide cija mudamlonjezaco, ndi kuti, Sadzakusowa munthu pamaso panga wakukhala pa mpando wacifumu wa Israyeli; pokhapo ngati ana ako asamalira njira yao, kuti ayende m'cilamulo canga, monga umo unayendera iwe pamaso panga.

17. Ndipo tsopano, Yehova Mulungu wa Israyeli, acitike mau anu amene munanena kwa Davide mtumiki wanu.

18. Koma kodi nzoona kuti Mulungu akhala ndi anthu pa dziko lapansi? taonani, thambo, inde m'mwambamwamba, sizifikira inu, koposa kotani nanga nyumba iyi ndaimanga?

19. Cinkana citero, labadirani pemphero la kapolo wanu, ndi pembedzero lace, Yehova Mulungu wanga, kumvera kupfuula ndi kupempha kwace, kumene kapolo wanu apempha pamaso panu;

2 Mbiri 6