2 Mbiri 6:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Solomo anati, Yehova anati kuti adzakhala mu mdima wandiweyani.

2. Koma ndakumangirani nyumba yokhalamo, malo okhazikika okhalamo Inu nthawi yosatha.

3. Ndipo mfumu inapotolokera nkhope yace, nidalitsa khamu lonse la Israyeli; ndi khamu lonse la Israyeli linaimirira.

4. Nati iye, Alemekezedwe Yehova Mulungu wa Israyeli, wakunena m'kamwa mwace ndi Davide atate wanga, nakwaniritsa: ndi manja ace, ndi kuti,

5. Kuyambira tsiku lakuturutsa Ine anthu anga m'dziko la Aigupto, sindinasankha mudzi uli wonse m'mafuko onse a Israyeli, kumangamo nyumba yokhalamo dzina langa, kapena kusankha munthu ali yense akhale kalonga wa anthu anga Israyeli;

6. koma ndinasankha Yerusalemu, kuti dzina langa likhale komweko; ndinasankhanso Davide akhale mfumu ya anthu anga Israyeli.

2 Mbiri 6