22. Namuka Hilikiya ndi iwo aja adawauza mfumu kwa Hulida mneneri wamkazi, mkazi wa Salumu mwana wa Tokati, mwana wa Hasire wosunga zobvala, amene anakhala m'Yerusalemu m'dera laciwiri, nanena naye mwakuti.
23. Ndipo iye ananena nao, Atero Yehova Mulungu wa Israyeli, Muuze munthuyo anakutumizani kwa ine,
24. Atero Yehova, Taonani, ndifikitsira malo ano ndi anthu okhala m'mwemo coipa, ndico matemberero onse olembedwa m'buku adaliwerenga pamaso pa mfumu ya Yuda;