2 Mbiri 34:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. anazipereka kwa amisiri a mitengo ndi omanga nyumba, agule miyala yosema, ndi mitengo ya mitanda yam'mwamba ndi yammunsi ya nyumbazi, adaziononga mafumu a Yuda.

12. Ndipo amunawo anacita nchitoyi mokhulupirika; ndi oikidwa awayang'anire ndiwo Yohati ndi Obadiya, Alevi, a ana a Merari; ndi Zekariya ndi Mesulamu, a ana a Akohati, kuifulumiza; ndi Alevi ena ali yense wa luso la zoyimbira,

13. Anayang'aniranso osenza akatundu, nafulumiza onse akugwira nchito ya utumiki uli wonse; ndi mwa Alevi munali alembi, ndi akapitao, ndi odikira.

14. Ndipo pakuturutsa ndarama zimene adalowa nazo ku nyumba ya Yehova, Hilikiya wansembe anapeza buku la cilamulo la Yehova mwa dzanja la Mose.

2 Mbiri 34