2 Mbiri 29:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Hezekiya analowa ufumu wace ali wa zaka makumi awiri mphambu zisanu, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi awiri mphambu zisanu ndi zinai; ndi dzina la mace ndiye Abiya mwana wa Zekariya.

2. Nacita iye zoongoka pamaso pa Yehova, monga umo monse adacitira Davide kholo lace.

3. Caka coyamba ca ufumu wace, mwezi woyamba, anatsegula pa makomo a nyumba ya Yehova, napakonzanso.

2 Mbiri 29