25. Ndi m'midzi iri yonse ya Yuda anamanga misanje ya kufukizira milungu yina, nautsa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa makolo ace.
26. Macitidwe ena tsono, ndi njira zace zonse, zoyamba ndi zotsiriza, taonanani, zilembedwa m'buku la mafumu a Yuda ndi Israyeli.
27. Ndi Ahazi anagona ndi makolo ace, namuika m'mudzi wa Yerusalemu; pakuti sanadza naye ku manda a mafumu a Israyeli; ndipo Hezekiya mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.