2 Mbiri 25:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo Amaziya anamemeza Ayuda, nawaika monga mwa nyumba za atate ao, atsogoleri a zikwi, ndi atsogoleri a mazana, ndiwo onse a Yuda ndi Benjamini; nawawerenga a zaka makumi awiri ndi mphambu, nawapeza amuna osankhika zikwi mazana atatu akuturukira kunkhondo, ogwira mkondo ndi cikopa.

6. Analemberanso ngwazi zamphamvu za m'Israyeli zikwi zana limodzi, kuwalipira matalente a siliva zana limodzi.

7. Koma anamdzera munthu wa Mulungu, kuti, Mfumu, khamu la nkhondo la Israyeli lisapite nanu; pakuti Yehova sakhala ndi Israyeli, sakhala ndi ana onse a Efraimu.

8. Koma ngati mumuka, citani, limbikani kunkhondo, Mulungu adzakugwetsani pamaso pa adani; pakuti Mulungu ali nayo mphamvu yakuthandiza ndi yakugwetsa.

9. Ndipo Amaziya anati kwa munthu wa Mulungu, Koma nanga titani nao matalente zana limodzi ndinapatsa ankhondo a Israyeli? Nati munthu wa Mulungu, Yehova ali nazo zoposa izi kukupatsani.

2 Mbiri 25