2 Mbiri 20:29-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Ndipo kuopsa kwa Mulungu kunagwera maufumu onse a m'maiko, pamene anamva kuti Yehova adayambana ndi adani a Israyeli.

30. Nucita bata ufumu wa Yehosafati; pakuti Mulungu wace anampumulitsira pozungulirapo.

31. Momwemo Yehosafati anakhala mfumu ya Yuda; anali wa zaka makumi atatu mphambu zisanu polowa ufumu wace, nakhala mfumu m'Yerusalemu zaka makumi awiri; ndi dzina la mace ndiye Azuba mwana wa Sili.

32. Ndipo anayenda m'njira ya Asa atate wace osapambukamo, nacita zoongoka pamaso pa Yehova.

33. Komatu misanje siinacotsedwa; popeza pamenepo anthu sadakonzere mitima yao kwa Mulungu wa makolo ao.

34. Macitidwe ena tsono adazicita Yehosafati, zoyamba ndi zotsiriza, taonani, zilembedwa m'buku la mau a Yehu mwana wa Hanani, wochulidwa m'buku la mafumu a Israyeli.

2 Mbiri 20