2 Mbiri 20:13-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo Ayuda onse anakhala ciriri pamaso pa Yehova, pamodzi ndi makanda ao, akazi ao, ndi ana ao.

14. Pamenepo mzimu wa Yehova unagwera Yahazieli mwana wa Zekriya, mwana wa Benaya, mwana wa Yetieli, mwana wa Mataniya, Mlevi, wa ana a Asafu, pakati pa msonkhano;

15. nati iye, Tamverani Ayuda inu nonse, ndi inu okhala m'Yerusalemu, ndi inu mfumu Yehosafati, atero nanu Yehova, Musaope musatenge nkhawa cifukwa ca aunyinji ambiri awa; pakuti nkhondoyi si yanu, koma ya Mulungu.

2 Mbiri 20