2 Mbiri 18:5-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pamenepo mfumu ya Israyeli anamemeza aneneri amuna mazana anai, nanena nao, Kodi timuke kunkhondo ku Ramoti Gileadi kapena ndileke? Ndipo anati, Kweraniko, pakuti Mulungu adzaupereka m'dzanja la mfumu.

6. Koma Yehosafati anati, Kulibenso kuno mneneri wa Yehova, kuti tifunsire kwa iye?

7. Ndipo mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Atsalanso munthu mmodzi, tifunsire Yehova kwa iye; koma ndimuda, pakuti sandinenera ine kanthu kokoma, koma zoipa nthawi zonse, ndiye Mikaya mwana wa Yimla. Nati Yehosafati, Isatero mfumu.

8. Pamenepo mfumu ya Israyeli inaitana mdindo, niti, Katenge msanga Mikaya mwana wa Yimla.

9. Mfumu ya Israyeli tsono ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anakhala yense pa mpando wacifumu wace, obvala zobvala zacifumu zao, nakhala pamalo poyera polowera pa cipata ca Samariya; ndi aneneri onse ananenera pamaso pao.

10. Ndipo Zedekiya mwana wa Kenana anadzisulira nyanga zacitsulo, nati, Atero Yehova, Ndi izi udzagunda Aaramu mpaka adatha psiti.

11. Ndi aneneri onse ananenera momwemo, ndi kuti, Kwerani ku Ramoti Gileadi, mudzapindulako; pakuti Yehova adzaupereka m'dzanja la mfumu.

12. Ndipo mthenga wakukaitana Mikaya ananena naye, ndi kuti, Taonani, mau a aneneri anenera mfumu cokoma ngati m'kamwa m'modzi; mau anu tsono akhaletu ngati amodzi a iwowa, nimunene cokoma.

13. Nati Mikaya, Pali Yehova, conena Mulungu wanga ndidzanena comweci.

14. Pamene anafika kwa mfumu, mfumu inanena naye, Mikaya timuke ku Ramoti Gileadi kunkhondo kodi, kapena ndileke? Nati iye, Kwerani, mudzacita mwai; ndipo adzaperekedwa m'dzanja lanu.

15. Ndipo mfumu inati naye, Ndikulumbiritse kangati kuti unene nane coonadi cokha cokha m'dzina la Yehova?

16. Nati iye, Ndinaona Aisrayeli onse obalalika pamapiri ngati nkhosa zopanda mbusa; nati Yehova, Awa alibe mbuye wao, abwerere yense ku nyumba yace mumtendere.

17. Ndipo mfumu ya Israyeli inati kwa Yehosafati, Sindinakuuzani kuti sadzandinenera zabwino koma zoipa?

18. Nati iye, Cifukwa cace tamvani mau a Yehova, Ndinaona Yehova alikukhala pa mpando wace wacifumu, ndi khamu lonse lakumwamba lirikuima pa dzanja lace lamanja, ndi pa dzanja lace lamanzere.

19. Nati Yehova, Adzamnyenga Ahabu mfumu ya Israyeli ndani, kuti akwereko, nagwe ku Ramoti Gileadi? Nati wina mwakuti, wina mwakuti.

20. Ndipo unaturuka mzimu, nuima pamaso pa Yehova, nuti, Ndidzamnyenga ndine. Ndipo Yehova, ananena nao, Ndi ciani?

21. Nuti uwu, Ndidzaturuka ndi kukhala mzimu wonama m'kamwa mwa aneneri ace onse. Nati Iye, Udzamnyengadi, nudzakhoza; turuka, ukatero kumene.

22. Ndipo tsono taonani, Yehova analonga mzimu wabodza m'kamwa mwa aneneri anu awa, nakunenetserani coipa Yehova.

23. Pamenepo Zedekiya mwana wa Kenana anayandikira, nampanda Mikaya patsaya, nati, Mzimu wa Yehova wandicokera bwanji kulankhula ndi iwe?

24. Nati Mikaya, Tapenya, udzaona tsiku lolowa iwe m'cipinda cam'kati kubisala.

25. Ndipo mfumu ya Israyeli inati, Mumtenge Mikaya, mukambweze kwa Amoni kazembe wa mudzi, ndi kwa Yoasi mwana wa mfumu;

2 Mbiri 18