2. Koma mau a Yehova anadza kwa Semaya munthu wa Mulunguyo, ndi kuti,
3. Lankhula ndi Rehabiamu mwana wa Solomo mfumu ya Yuda ndi Benjamini, ndi kuti,
4. Atero Yehova, Musamuka kukayambana ndi abale anu, bwererani yense ku nyumba yace; pakuti cinthu ici cifuma kwa Ine. Ndipo anamvera mau a Yehova, nabwerera osakayambana ndi Yerobiamu.
5. Ndipo Rehabiamu anakhala m'Yerusalemu, namanga midzi yolimbikiramo m'Yuda.