16. Ndipo akuwatsata iwo anadza ku Yerusalemu, ocokera m'mafuko onse a Israyeli, iwo akupereka mitima yao kufuna Yehova Mulungu wa Israyeli, kudzaphera Yehova Mulungu wa makolo ao nsembe.
17. Momwemo analimbikitsa ufumu wa Yuda, nalimbikitsa Rehabiamu, mwana wa Solomo zaka zitatu; pakuti anayenda m'njira ya Davide ndi Solomo zaka zitatu.
18. Ndipo Rehabiamu anadzitengera mkazi Mahalati, mwana wamkazi wa Yerimoti mwana wa Davide, ndi wa Abihaili mwana wamkazi wa Eliabu mwana wa Jese;
19. ndipo anambalira ana, Yeusi, ndi Semariya, ndi Zahamu.