2 Mafumu 5:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Pamenepo mfumu ya Aramu inati, Tiye, muka, ndidzatumiza kalata kwa mfumu ya Israyeli. Pamenepo anacoka, atatenga siliva: matalente khumi, ndi golidi masekeli zikwi zisanu ndi cimodzi, ndi zobvala zakusintha khumi.

6. Ndipo anafika kwa mfumu ya Israyeli ndi kalata, wakuti, Pakulandira kalata uyu, taonani, ndatumiza Namani mnyamata wanga kwa inu, kuti mumciritse khate lace.

7. Ndipo kunali atawerenga kalatayu mfumu ya Israyeli, anang'amba zobvala zace, nati, Ngati ndine Mulungu, kupha ndi kubwezera moyo, kuti ameneyo atumiza kwa ine kumciritsa munthu khate lace? pakuti dziwani, nimupenye, kuti alikufuna cifukwa pa ine.

8. Koma kunali, pamene Elisa munthu wa Mulungu anamva kuti mfumu ya Israyeli adang'amba zobvala zace, anatumiza mau kwa mfumu, ndi kuti, Mwang'amba zobvala zanu cifukwa ninji? Adzetu kwa ine, ndipo adzadziwa kuti muli mneneri m'Israyeli.

2 Mafumu 5