2 Mafumu 5:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Namani kazembe wa khamu la nkhondo la mfumu ya Aramu anali munthu womveka pamaso pa mbuyace, ndi waulemu; popeza mwa iye Yehova adapulumutsa Aaramu; ndiyenso ngwazi, koma wakhate.

2. Ndipo Aaramu adaturuka magulu magulu, nabwera nalo m'ndende buthu locokera ku dziko la Israyeli, natumikira mkazi wa Namani iyeyu,

3. Nati uyu kwa mbuyace wamkazi, Mbuye wanga akadakhala kwa mneneri ali m'Samariya, akadamciritsa khate lace.

2 Mafumu 5