2 Mafumu 4:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo anati, Nyengo yino caka cikudzaci udzafukata mwana wamwamuna. Koma anati, lai, mbuyanga, munthu wa Mulungu, musanamiza mdzakazi wanu.

17. Ndipo mkaziyo anaima, naona mwana wamwamuna nyengo yomweyo caka cimene cija Elisa adanena naye.

18. Ndipo atakula mwanayo, linadza tsiku lakuti anaturuka kumka kwa atate wace, ali kwa omweta tirigu.

19. Natikwa atate wace, Mutu wanga, mutu wanga! Pamenepo anati kwa mnyamata, Umnyamule umuke naye kwa amace.

2 Mafumu 4